Ayimitsa mkulu wa bungwe losunga zakudya

Mkulu wa bungwe losunga zakudya mdziko la National Food Reserve Agency  muno a Brenda Kayongo awayimitsa kaye pa udindo wawo.

Wa pambando wa komiti  yoyendetsa bungweli a Dennis Kalekeni ati mayi Kayongo adawayimitsa malinga ndi nkhani yakusowa kwa ma lole 13 a chimanga mchaka cha 2022.

A Kalekeni ati komiti  yawo yapeza kuti akulu akulu ena a bungweli sanagwire ntchito yawo bwino nchifukwa chimanga chidasowa.

Ma lole  13 a Smollet Kachere omwe ndi mmodzi mwa akuluakulu a chipani cholamula cha Malawi Congress (MCP) adasowa  ngati mmene galeta la Eliya mu bayibulo  linasowela ndipo mpaka pano a Kachere safotokoza kuti adanka kuti.

A Kachere atasowetsa ma lole adauza bungweli liwalipile K112 million kuwonjezelapo zomwe zinali zodabwitsa ntundu wonse.

A Kachere polankhula ku nyumba ya malamulo pomwe anayitanidwa kuti afotokoze za nkhaniyi, adaulula kuti bungwe la Admaki  lakhala likunamiza a Malawi kuti lili ndi matani 38,000 pomwe chimangacho chidabedwa.

“Kulibeko ma tani amakambidwawo, afunseni akulozeleni,” a Kachere adauza a tolankhani

Mpaka pano palibe anayankhapo zomwe ananena a Kachere.

Mtengo wa chimanga pano wakwela kowospya mwakuti mmadela ena monga mboma la Nsanje chimanga chili pa K35,000 thumba la ma kilogalamu  fifite. 

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *