Malawi’s information Minister attacks Journalist

Information and Technology  Minister Gospel Kazako on Tuesday verbally attacked renowned Times TV presenter Brian Banda.

In a shocking tirade as the reporter tried to probe who is in charge of the country after  President President Lazarus Chakwera, Kazako and two senior Minister told the public they were not aware of the arrest of ACB Director General Martha Chizuma.

Kazako did not answer the question but resorted to innuendos.

Hon. Gospel Kazako: Minister of Information and Digitization

The Investigator transcribed the interview 

Brian Banda: Timafuna tilandile omwe amalankhulila Boma ili anduna Gospel Kazako tikulandileni madzulo ano

Gospel Kazako: Zikomo Kwambiri

Brian Banda: Kunjaku Anthu akunena kuti iyii yakuphulikilani nkhaniyi, mumadziwa koma mwina mmangoyetsa madzi (you were testing the waters) nde yaphulika ndemufuna muoneke ngati kuti simmadziwa funso lofunikila kwambiri nali ndani akuonerela(Who is in control) ndani angadzuke lero ndi lero kulamula apolice kanjateni a Martha chizuma pomwe nonse kuphatikizilapo a president musakudziwa nchifukwa chake ndafunsa tili pabwino mdziko muno ndufuna muyankhe funsoli anduna (Who is in control) ndani akulamula ndani angalamule apolice kukachita zimenezi.

Gospel Kazako: nsanafike kumeneko

Brian Banda: Eya

Gospel Kazako: Kunena kuti chinthuchi chatiphulikila komanso kugwilitsa ntchito mau onena kuti anthu akuti anthu amatha kunena zinthu zosiyanasiyana

Brian Banda: iyayi ndimangofuna ndinene kuti mwina simukuziwa zimene anthu akunena kunjaku

Gospel Kazako: Ayi ayi chifukwa tikapanga choncho ndekuti tilakwisa

Brain banda: (mhm)

Gospel Kazako: ndofuna tisate nkhaniyi

Brian Banda: (mhm)

Gospel Kazako: ndofuna tisate nkani chifukwa anthu amatha kunena zinthu zambiri anthu amatha kunenana zinthu zokunyoza iweyo brian simene sizili zoona, a brian amagwilitsa ncthito certificate yam’bale wao anthu amanena zimenezi, abrian sadapiite ku school adalekeza form two, a biran izi a brian izi  anthu amanena zinthu zosiyana siyana tinene kuti zinthuzi nzoona kuti mmagwilitsa ncthito pepala yam’bale wanu ayi

Brian Banda: Ndufuna tikambilane nkhani zeni zeni

Gospel Kazako: Ayi ayi nduziwa iyiso ndinkhani mwaimodzi yazokambilana

Brian Banda: ndufuna muyankhe Funso ililii ndani akuonerela (who is in Control)

Gospel Kazako: Iyinsoo ilimmodzi mwankhani yomwe tukambilana chifukwa iweee nde wabweresa nkhani yoti anthu akuti

Brian Banda: Iyayi iyayi  

Gospel Kazako: ineso ndukupasa chisanzo kuti anthuso amanena kuti inu mulibe pepala la fomu folo (4) amangonena

Brian Banda: iyayi izo ndi nkhambakamwa chabe

Gospel Kazako: inde mongofananizila izonso zikhozakukhala chimodzimodzi kuti anthu akhoza kungonena zinthu nanga mufuna mukhulupilile zinthu zomwe anthu amakunenezelani zainu pokhapokha zikhale zoona tipitilize motere mofanana.

Brian Banda: Funso langa ndilakuti akuonelela ndindani (Who is in Control)

Gospel Kazako: ilo nde linali funso mukadandifunsa.

 There has been mixed reaction from the public

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *